[Lyrics]Mr Praise – Nthawi ft SayNewz
![[Lyrics]Mr Praise – Nthawi ft SayNewz](https://i0.wp.com/zambuye.com/wp-content/uploads/2022/01/Mista-Praise-Nthawi-ft-Saynewz-mp3-image.jpg?resize=850%2C560&ssl=1)
Nthawi by Mr Praise & SayNewz Lyrics
Verse 1
Palibe olo mmozi akudziwa tsikulo/
Kuti uzakhala Masana kapenanso madzulo/
Kudabwa mzako wapita umacheza naye dzulo/
Kukanika kumvetsa ngati zachitika mtulo/
Ndiye mmene zinalili mmatsiku a Noah/
Ndimeneso zilili matsiku anowa/
Ma plans aukwati ali mkati mophikidwa/
Mmalo mokwatilana mmoziyo nkukwatulidwa/
Ma signs aonetsa nthawi yayandikira/
Mtundu kuukirana, njala komanso nthenda/
Kupanga legalise zomwe zili zoipa..mau ananena kale pano zikuchitika/
Nthawi ikuyenda ndipo ili close/
Kutembenuka mtima si tomorrow of course/
Nthawi ndi yomweyi mulandire upulumuke/
Mmanja mwake ukhala safe sangalore upulumuke
Chorus
Kudzakhala chimwemwe kwa onse oyera mtima/
Kudzakhala chimwemwe kwa onse oyera mtima/
Adzawonana ndi Mbuye wao/
Adzawonana, ndi Mbuye Yesuu!
Verse 2
Sakubwera Ngati mwana ayi akubwera ndi Glory/
Sakubwera kuzakhala kma kuti azakolore/
Anabwera kale kuti ochimwa onse apulumuke/
But this time akubwera olungama tinyamuke/
Zili ngati mayeso ofunika kukonzekera/
Kuyamba study tsiku lomwelo sizikuyendera/
Iwe nzotheka kupulumuka osaziyeza taya ruler/
Look at us talandira yesu mphasa tayalura /
Tidzasangalala heavy ndi maso kuzamupenya/ Tidzamuona reality osatiso masomphenya/
Ndiye ndifunse kodi inu mumakhalira ndani/
Ntambasule kodi moyo wanu mwini wake ndi ndani?/
Yesu ndiye wosunga moyo tsegula mtima nku surrender/
Kumwamba ndikokoma yemwe amafuna azasale nda?
Chorus
Kudzakhala chimwemwe kwa onse oyera mtima/
Kudzakhala chimwemwe kwa onse oyera mtima/
Adzawonana ndi Mbuye wao/
Adzawonana, ndi Mbuye Yesuu!
Verse 3
Kodi m’bale wakonzeka?
Kulandira Moyo/
Kodi M’bale wakonzeka?
Kukumana naye/
Yesu akubwera, posachedwa/
Mfumu ikubweraa, posachedwa/
Hallelujah!
Back to chorus